Kumudziwa Imam Sadiq (A.s) mwachidule (3)

Nthawi ya Imam Sadiq (A.S) ndi nthawi yomwe atsogoleri ambiri a ulamuliro opondereza adaphedwa ndi asilamu. Izi ziri choncho chifukwa chakuti anthu adapeza chiphunzitso polimbana ndi anthu opondereza kuchokera kwa Imam Husein (A.S) pomwe adalimbana ndi Yazid. Kuponderezedwa kwa njira ya chiwongoko kudayambika nthawi yomwe Mtumiki wathu okondedwa adamwalira kufikira pomwe Imam Mahdi (AJ) akubisidwa ndi Mulungu pofuna kumuteteza kuchokera kwa adani ndi anthu opondereza. Imam Sadiq (A.S) adatenga gawo poteteza Chisilamu cheni cheni polimbana ndi magulu osocheretsa.

AttachmentSize
File b34757c318a877e29fee21bf54f72b3f.mp430.87 MB

Add new comment