Choonadi cha banja mu Chisilamu

 

Choonadi cha  banja  mu Chisilamu

 Kodi  choona  cheni cheni  cha  banja  muchisilamu  ndi  chiti?
Komanso  ndichifukwa  chani  chisilamu  chimalimbikitsa  nkhani  ya  banja?
Sheikh  Allamah  Muhammad  Taqi  Ja’afari  pofuna  kuyankha  funso  lomwe  mkulu  wina  yemwe  ndi  Philosopher  waku  Europe  adamufunsa  kuti  kodi  ndichifukwa  chiyani  chisilamu  chimalimbikitsa  banja?  Adati:  “ banja  ndi  njira  imodzi  yomwe   mtundu  wa  anthu  umapitilira”.
Mu banja  mumapezeka  zinthu  zabwino  zambiri   monga izi:
1.  Chikwaniritso.
Munthu  wina  aliyense  ndioperewera  choncho  amakhala  akutaka-taka  cholinga  choti  athe  kupeza  chinthu  chomwe  chimukwaniritse. Mnyamata  amakhala  akufunafuna   mpata  oti  athe  kukhala oziimira  yekha  pamaganizo ndikuthetsa  mavuto  ambiri  omwe  amakhala  nawo, pachifukwa  ichi  amakhala  akufunafuna  mkazi  oyenera  kuti  athe  kumanga  naye  banja  ndikumakhala. Kudzera  mubanja  limeneli iye  amapeza  chikwaniritso  chomwe  amachisowekera  nthawi  yomwe  adali  yekha.
Sheikh  Mutwahari  panganiyi  adanena  kuti:
Kukhala  ndibanja  ndichifuniro  cha  tsogolo la  ena  chifukwa  kuchokera  mubanja  limeneli  anthu ena  amapeza  chisamaliro  ndi tsogolo  labwino , ichi chitha  kukhala  chimodzi  mwa  zifukwa  zomwe   chisilamu  chimalimbikitsira  banja. Mu banja  ndi momwe  munthu  amapeza  umunthu  wake. Mu banja  munthu amakumana  ndi  zinthu  zomwe  zimampangitsa  kuti  akhale  okwanira. Munthu  amakhala  ndikutha  kokhala  umoyo  wapagulu (society).
2.  Mpumulo.
Chinthu  chomwe  chili  chofunikira  kwambiri  m’banja  ndi  nkhani  ya  mpumulo   chomwe  ndi chinthu chomwe  chili  mu  chilengedwe  cha  munthu  pomwe   Mulungu akunena  kuti:
«وَ مِنْ آياتِهِ أَنْ خَلَقَ لَكُمْ مِنْ أَنْفُسِكُمْ أَزْواجاً لِتَسْكُنُوا إِلَيْها وَجَعَلَ بَيْنَكُمْ مَوَدَّةً وَرَحْمَةً إِنَّ فِي ذلِكَ لآَياتٍ لِقَوْمٍ يَتَفَكَّرُونَ(روم/21):
((China mwa  zionetsero  zake ndikuti  adalenga  akazi  kuchokera  mwa inu  nokha   ndicholinga  choti  muzipezeramo  mpumulo  ndipo  Mulungu adaika  mkati  mwakemo  chikondi  ndi chisoni,  mu zinthu  izi   muli  zionetsero  kwa  anthu   omwe ali  oganiza)).
Mu ayayi  tamva  kuti  mkazi  ndinjira  yomwe  mwamuna  amapezera  mpumulo. Nthawi  yomwe  munthu  amakhala  wachinyamata  amakhala  kuti  alibe  munthu  ocheza  ndikusewera  naye   koma  akakwatira  amakhala  kuti tsopano  ali  ndi  omuchotsa  kusungulumwa,  inde  banja  ndi  mtendere  ochokera  kwa  Mulungu. Anthu  omwe  ali  odziwa   nkhani  za  science  ndi  humanity  adavomereza  kuti  kukumana  malo  amodzi  kwa  mwamuna  ndi  mkazi kumabweretsa  mtendere  ndi  kuyenda  bwino  kwa  nzeru  mthupi  la  munthu, ndipo  kupanda  kutero  kumabweretsa  vuto  mthupi  ndi  nzeru  za  munthu.
3.  Kupitiliza  mtundu.
Ubwino  wina  wa  Banja  oti  ana  akabadwa  ana  amenewa  amapitiliza  mtundu  wa    anthu   zomwe zili  zinthu  zofunikira  pa dziko  lapansi. Nkhani yopitiliza  mtundu  imeneyi  sifunikira kuitenga  ngati  nkhani  yopanda  pake  monga  momwe  anthu  amaganizira  posaikira  mtima  pa  banja  ndikumapanga  zinthu  zosalongosoka  zomwe  mapeto  ake   zitha  kuthetsa mtundu,  chifukwa  cholinga  chopangira  ndiye kuti  mtundu  upitilire  kuti  anthu  apezekemo.  Banja  likakhala  labwino  ndiye  kuti  limatulutsa  ana  abwino  omwe  amakhala  opembedza, angwiro,oyera  mtima   ndi ogwira  ntchito  zabwino,  izi  ndizinthu  zomwe  Mulungu  akuzifuna  kuchokera  kwa  anthu.Mukuona  kwa  Chisilamu  banja  likakhala  ndi  mwana  wabwino  ndi  wangwiro  zimatengedwa  kuti  makolo  awiri  amwanayu  agwira  ntchito yoyera  ndi yabwino,  ndipo  mwana ameneyu  adzakhala  ofunikira  padziko  lapansi  nditsiku  lomaliza.
Mtumiki(s.a.a.w)  polimbikitsa  nkhaniyi  adati: (( Kodi  pali  vuto  lanji  kuti  munthu  okhulupirira  akwatire  mkazi  kutheka  Mulungu  kudzera  mwa  mkazi  ameneyu  adzampatsa  iye  mwana  wabwino  yemwe  ndikulankhula  kwake  mau  oti ((Palibe wina  omupembedza  muchoonadi  koma  Mulungu  mmodzi  yekha))  angagwedeze  dziko.
Banja  limapangitsa  kuti  munthu  akhale  mwaufulu  ndi  mopanda  mantha.
Banja  ndi kampani  yopititsira  patsogolo  mtundu  wa  anthu.
Banja  ndi pothawira  ndi  pobisala  pa  mwamuna  ndi  mkazi.
Banja  ndi  limapangitsa  munthu  kuti  cholinga  chokhalira  pagulu  achimvetsetse.
Banja  limapangitsa  kuti  umoyo  wapagulu  ulimbikitsidwe.
Banja  limapangitsa  kuti  vuto  lomwe  adali  nalo  lofuna  mkazi lithetsedwe  mokwanira.
Banja  limateteza  munthu  kuchokera  kumatenda  a pa  thupi  ndi mmutu.
Banja  limateteza  munthu  kuchokera  kuzochitika  zotailira  monga  chigololo ndi  zina.
Pomaliza  ndipemphe  Asilamu  onse  kuti  alitenge  banja  kukhala  chinthu  chofunikira  kwambiri  muchipembedzo  chathu cha  Chisilamu. Amene  sadakwatire  ndibwino  kuti akwatire Mulungu  amudalitsa,  amene  adakwatira  ayenera  kulemekeza  banja  lake  ndikukondana  pakati  pawo  kuti  ubwino  wa banja  upezeke.
Wassalam  alaikum  warahamatullah  ta’ala  wa barakatuh.

Add new comment